[ad_1]
Chipani cha Alliance for Democracy (Aford) chati chili ndi chikhulupiliro kuti chidzapambana chikadzaima pa chokha pa chisankho cha mtsogoleri wa dziko cha chaka cha mawa.
Wofalitsa nkhani za chipanichi a Amatullah Annie Maluwa auza Nyasatimes kuti kwa zaka zitatu tsopano chipanichi chakula mphamvu zimene zikupereka chirimbikitso kuti chidzaime pa chokha.
A Maluwa ati kutuluka kwa anthu ena mchipanichi ndi chitsimikizo kuti m’chipanichi muli demokalase ndipo anthu ena akhale akulowanso mchipanichi.
Posachedwapa, amene adali mlembi wamkulu wa chipanichi a Elias Wakuda Kamanga adatuluka mchipanichi ndi kulowa chipani chomwe chidayambitsidwa kumene cha National Development Party chomwe chikusogozedwa ndi a Frank Mwenifumbo
Aford inkadzudzula a Kamanga kuti ankapanga ndale za umthira kuwiri zomwe iwo eni adakana.
Follow and Subscribe Nyasa TV :
Sharing is caring!
[ad_2]
Source link